Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Masalmo 71:21-24 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

21. Mundionjezere ukulu wanga,Ndipo munditembenukire kundisangalatsa,

22. Ndiponso ndidzakuyamikani ndi cisakasa,Kubukitsa coonadi canu, Mulungu wanga;Ndidzakuyimbirani Nyimbo ndi zeze,Ndinu Woyerayo wa Israyeli.

23. Milomo yanga idzapfuula mokondwera poyimbira Inu Nyimbo;Inde, moyo wanga umene munaombola.

24. Lilime langa lomwe lidzalankhula za cilungamo canu tsiku lonse:Pakuti ofuna kundicitira coipa acita manyazi, nadodoma.

Werengani mutu wathunthu Masalmo 71