Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Masalmo 7:7-15 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

7. Ndipo ukuzingeni msonkhano wa anthu;Ndipo pamwamba pao mubwerere kumka kumwamba.

8. Yehova aweruza anthu mlandu:Mundiweruze, Yehova, monga mwa cilungamo canga, ndi ungwiro wanga uli mwa ine.

9. Ithe mphulupulu ya anthu oipa, ndikupemphani, koma wolungamayo mumkhazikitse:Pakuti woyesa mitima ndi imso ndiye Mulungu wolungama.

10. Cikopa canga ciri ndi Mulungu, Wopulumutsa oongoka mtima.

11. Mulungu ndiye Woweruza walungama,Ndiye Mulungu wakukwiya masiku onse.

12. Akapanda kutembenuka munthu, Iye adzanola lupanga lace;Wakoka uta wace, naupiringidza.

13. Ndipo anamkonzera zida za imfa;Mibvi yace aipanga ikhale yansakali,

14. Taonani, ali m'cikuta ca zopanda pace;Anaima ndi cobvuta, nabala bodza.

15. Anacita dzenje, nalikumba,Nagwa m'mbuna yomwe anaikumba.

Werengani mutu wathunthu Masalmo 7