3. Yehova Mulungu wanga, ngati ndacita ici;Ngati m'manja anga muli cosalungama;
4. Ngati ndambwezera coipa iye woyanjana ndine;(Inde, ndamlanditsa wondisautsa kopanda cifukwa);
5. Mdani alondole moyo wanga, naupeze;Naupondereze pansi moyo wanga,Naukhalitse ulemu wanga m'pfumbi.
6. Ukani Yehova mu mkwiyo wanu,Nyamukani cifukwa ca ukali wa akundisautsa:Ndipo mugalamukire ine; mwalamulira ciweruzo.
7. Ndipo ukuzingeni msonkhano wa anthu;Ndipo pamwamba pao mubwerere kumka kumwamba.
8. Yehova aweruza anthu mlandu:Mundiweruze, Yehova, monga mwa cilungamo canga, ndi ungwiro wanga uli mwa ine.