Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Masalmo 7:10-17 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

10. Cikopa canga ciri ndi Mulungu, Wopulumutsa oongoka mtima.

11. Mulungu ndiye Woweruza walungama,Ndiye Mulungu wakukwiya masiku onse.

12. Akapanda kutembenuka munthu, Iye adzanola lupanga lace;Wakoka uta wace, naupiringidza.

13. Ndipo anamkonzera zida za imfa;Mibvi yace aipanga ikhale yansakali,

14. Taonani, ali m'cikuta ca zopanda pace;Anaima ndi cobvuta, nabala bodza.

15. Anacita dzenje, nalikumba,Nagwa m'mbuna yomwe anaikumba.

16. Cobvuta cace cidzambwerera mwini,Ndi ciwawa cace cidzamgwera pakati pamutu pace.

17. Ndidzayamika Yehova monga mwa cilungamo cace;Ndipo ndidzayimbira Yehova Wam'mwambamwamba.

Werengani mutu wathunthu Masalmo 7