Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Masalmo 69:29-34 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

29. Koma ine ndine wozunzika ndi womva zowawa;Cipulumutso canu, Mulungu, cindikweze pamsanje.

30. Ndidzalemekeza dzina la Mulungu ndi kuliyimbira,Ndipo ndidzambukitsa ndi kumyamika.

31. Ndipo cidzakomera Yehova koposa ng'ombe,Inde mphongo za nyanga ndi ziboda,

32. Ofatsa anaciona, nakondwera:Ndipo inu, ofuna Mulungu, mtima wanu ukhale ndi moyo.

33. Pakuti Yehova amvera aumphawi,Ndipo sapeputsa am'ndende ace.

34. Zakumwamba ndi dziko lapansi zimlemekeze,Nyanja ndi zonse zoyenda m'mwemo;

Werengani mutu wathunthu Masalmo 69