Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Masalmo 69:21-32 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

21. Ndipo anandipatsa ndulu ikhale cakudya canga;Nandimwetsa vinyo wosasa pomva ludzu ine.

22. Gome lao likhale msampha pamaso pao;Pokhala ndi mtendere iwo, likhale khwekhwe.

23. M'maso mwao mude, kuti asapenye;Ndipo munjenjemeretse m'cuuno mwao kosalekeza.

24. Muwatsanulire mkwiyo wanu, Ndipo moto wa ukali wanu uwagwere.

25. Pokhala pao pakhale bwinja;M'mahema mwao musakhale munthu.

26. Pakuti alondola amene Inu munampanda;Ndipo akambirana za zowawa zao za iwo amene munawalasa.

27. Onjezani mphulupulu pa mphulupulu zao;Ndipo asafikire cilungamo canu.

28. Afafanizidwe m'buku lamoyo,Ndipo asalembedwe pamodzi ndi olungama,

29. Koma ine ndine wozunzika ndi womva zowawa;Cipulumutso canu, Mulungu, cindikweze pamsanje.

30. Ndidzalemekeza dzina la Mulungu ndi kuliyimbira,Ndipo ndidzambukitsa ndi kumyamika.

31. Ndipo cidzakomera Yehova koposa ng'ombe,Inde mphongo za nyanga ndi ziboda,

32. Ofatsa anaciona, nakondwera:Ndipo inu, ofuna Mulungu, mtima wanu ukhale ndi moyo.

Werengani mutu wathunthu Masalmo 69