21. Ndipo anandipatsa ndulu ikhale cakudya canga;Nandimwetsa vinyo wosasa pomva ludzu ine.
22. Gome lao likhale msampha pamaso pao;Pokhala ndi mtendere iwo, likhale khwekhwe.
23. M'maso mwao mude, kuti asapenye;Ndipo munjenjemeretse m'cuuno mwao kosalekeza.
24. Muwatsanulire mkwiyo wanu, Ndipo moto wa ukali wanu uwagwere.
25. Pokhala pao pakhale bwinja;M'mahema mwao musakhale munthu.
26. Pakuti alondola amene Inu munampanda;Ndipo akambirana za zowawa zao za iwo amene munawalasa.
27. Onjezani mphulupulu pa mphulupulu zao;Ndipo asafikire cilungamo canu.
28. Afafanizidwe m'buku lamoyo,Ndipo asalembedwe pamodzi ndi olungama,
29. Koma ine ndine wozunzika ndi womva zowawa;Cipulumutso canu, Mulungu, cindikweze pamsanje.
30. Ndidzalemekeza dzina la Mulungu ndi kuliyimbira,Ndipo ndidzambukitsa ndi kumyamika.