Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Masalmo 69:2-12 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

2. Ndamira m'thope lozama, lopanda poponderapo;Ndalowa m'madzi ozama, ndipo cigumula candimiza.

3. Ndalema ndi kupfuula kwanga; kum'mero kwauma gwa:M'maso mwanga mwada poyembekeza Mulungu wanga.

4. Ondida kopanda cifukwa acuruka koposa tsitsi la pamutu panga;Ofuna kunditha, ndiwo adani anga monama, ali ndi mphamvu:Pamenepo andibwezetsa cosafunkha ine.

5. Mulungu, mudziwa kupusa kwanga;Ndipo kutsutsika kwanga sikubisikira Inu.

6. Iwo akuyembekeza Inu, Ambuve Yehova wa makamu, asacite manyazi cifukwa ca ine:Iwo ofuna Inu, Mulungu wa Israyeli, asapepulidwe cifukwa ca ine.

7. Pakuti ndalola cotonza cifukwa ca Inu:Cimpepulo cakuta nkhope yanga,

8. Abale anga andiyesa mlendo,Ndi ana a mai wanga andiyesa wa mtundu wina.

9. Pakuti cangu ca pa nyumba yanu candidya;Ndi zotonza za iwo otonza Inu zandigwera ine.

10. Ndipo ndinalira pa kusala kwa moyo wanga,Koma uku kunandikhalira cotonza.

11. Ndipo cobvala canga ndinayesa ciguduli,Koma amandiphera mwambi.

12. Okhala pacipata akamba za ine; Ndipo oledzera andiyimba.

Werengani mutu wathunthu Masalmo 69