Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Masalmo 69:17-31 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

17. Ndipo musabisire nkhope yanu mtumiki wanu;Pakuti ndisautsika ine; mundiyankhe msanga.

18. Yandikizani moyo wanga, ndi kuuombola;Ndipulumutseni cifukwa ca adani anga,

19. Mudziwa cotonza canga, ndi manyazi anga, ndi cimpepulo canga:Akundisautsa ali pamaso panu,

20. Cotonza candiswera mtima, ndipo ndidwala ine;Ndipo ndinayembekeza wina wondicitira cifundo, koma palibe;Ndinayembekeza onditonthoza mtima, osawapeza.

21. Ndipo anandipatsa ndulu ikhale cakudya canga;Nandimwetsa vinyo wosasa pomva ludzu ine.

22. Gome lao likhale msampha pamaso pao;Pokhala ndi mtendere iwo, likhale khwekhwe.

23. M'maso mwao mude, kuti asapenye;Ndipo munjenjemeretse m'cuuno mwao kosalekeza.

24. Muwatsanulire mkwiyo wanu, Ndipo moto wa ukali wanu uwagwere.

25. Pokhala pao pakhale bwinja;M'mahema mwao musakhale munthu.

26. Pakuti alondola amene Inu munampanda;Ndipo akambirana za zowawa zao za iwo amene munawalasa.

27. Onjezani mphulupulu pa mphulupulu zao;Ndipo asafikire cilungamo canu.

28. Afafanizidwe m'buku lamoyo,Ndipo asalembedwe pamodzi ndi olungama,

29. Koma ine ndine wozunzika ndi womva zowawa;Cipulumutso canu, Mulungu, cindikweze pamsanje.

30. Ndidzalemekeza dzina la Mulungu ndi kuliyimbira,Ndipo ndidzambukitsa ndi kumyamika.

31. Ndipo cidzakomera Yehova koposa ng'ombe,Inde mphongo za nyanga ndi ziboda,

Werengani mutu wathunthu Masalmo 69