Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Masalmo 69:15-28 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

15. Cigumula cisandifotsere,Ndipo cakuya cisandimize;Ndipo asanditsekere pakamwa pace pa dzenje.

16. Mundiyankhe Yehova; pakuti cifundo canu ncokoma;Munditembenukire monga mwa unyinji wa nsoni zokoma zanu.

17. Ndipo musabisire nkhope yanu mtumiki wanu;Pakuti ndisautsika ine; mundiyankhe msanga.

18. Yandikizani moyo wanga, ndi kuuombola;Ndipulumutseni cifukwa ca adani anga,

19. Mudziwa cotonza canga, ndi manyazi anga, ndi cimpepulo canga:Akundisautsa ali pamaso panu,

20. Cotonza candiswera mtima, ndipo ndidwala ine;Ndipo ndinayembekeza wina wondicitira cifundo, koma palibe;Ndinayembekeza onditonthoza mtima, osawapeza.

21. Ndipo anandipatsa ndulu ikhale cakudya canga;Nandimwetsa vinyo wosasa pomva ludzu ine.

22. Gome lao likhale msampha pamaso pao;Pokhala ndi mtendere iwo, likhale khwekhwe.

23. M'maso mwao mude, kuti asapenye;Ndipo munjenjemeretse m'cuuno mwao kosalekeza.

24. Muwatsanulire mkwiyo wanu, Ndipo moto wa ukali wanu uwagwere.

25. Pokhala pao pakhale bwinja;M'mahema mwao musakhale munthu.

26. Pakuti alondola amene Inu munampanda;Ndipo akambirana za zowawa zao za iwo amene munawalasa.

27. Onjezani mphulupulu pa mphulupulu zao;Ndipo asafikire cilungamo canu.

28. Afafanizidwe m'buku lamoyo,Ndipo asalembedwe pamodzi ndi olungama,

Werengani mutu wathunthu Masalmo 69