Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Masalmo 69:11-19 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

11. Ndipo cobvala canga ndinayesa ciguduli,Koma amandiphera mwambi.

12. Okhala pacipata akamba za ine; Ndipo oledzera andiyimba.

13. Koma ine, pemphero langa liri kwa Inu, Yehova, m'nyengo yolandirika;Mulungu, mwa cifundo canu cacikuru,Mundibvomereze ndi coonadi ca cipulumutso canu.

14. Mundilanditse kuthope, ndisamiremo:Ndilanditseni kwa iwo akundida, ndi kwa madzi ozama.

15. Cigumula cisandifotsere,Ndipo cakuya cisandimize;Ndipo asanditsekere pakamwa pace pa dzenje.

16. Mundiyankhe Yehova; pakuti cifundo canu ncokoma;Munditembenukire monga mwa unyinji wa nsoni zokoma zanu.

17. Ndipo musabisire nkhope yanu mtumiki wanu;Pakuti ndisautsika ine; mundiyankhe msanga.

18. Yandikizani moyo wanga, ndi kuuombola;Ndipulumutseni cifukwa ca adani anga,

19. Mudziwa cotonza canga, ndi manyazi anga, ndi cimpepulo canga:Akundisautsa ali pamaso panu,

Werengani mutu wathunthu Masalmo 69