1. Ndipulumutseni Mulungu;Pakuti madzi afikira moyo wanga.
2. Ndamira m'thope lozama, lopanda poponderapo;Ndalowa m'madzi ozama, ndipo cigumula candimiza.
3. Ndalema ndi kupfuula kwanga; kum'mero kwauma gwa:M'maso mwanga mwada poyembekeza Mulungu wanga.
4. Ondida kopanda cifukwa acuruka koposa tsitsi la pamutu panga;Ofuna kunditha, ndiwo adani anga monama, ali ndi mphamvu:Pamenepo andibwezetsa cosafunkha ine.
5. Mulungu, mudziwa kupusa kwanga;Ndipo kutsutsika kwanga sikubisikira Inu.
6. Iwo akuyembekeza Inu, Ambuve Yehova wa makamu, asacite manyazi cifukwa ca ine:Iwo ofuna Inu, Mulungu wa Israyeli, asapepulidwe cifukwa ca ine.
7. Pakuti ndalola cotonza cifukwa ca Inu:Cimpepulo cakuta nkhope yanga,
8. Abale anga andiyesa mlendo,Ndi ana a mai wanga andiyesa wa mtundu wina.
9. Pakuti cangu ca pa nyumba yanu candidya;Ndi zotonza za iwo otonza Inu zandigwera ine.