2. Kuti ndione mphamvu yanu ndi ulemerero wanu,Monga ndinakuonani m'malo oyera.
3. Pakuti cifundo canu ciposa moyo makomedwe ace;Milomo yanga idzakulemekezani.
4. Potero ndidzakuyamikani m'moyo mwanga;Ndidzakweza manja anga m'dzina lanu.
5. Mudzakhutitsa moyo wanga ngati ndi mafuta ndi zonona;Ndipo pakamwa panga ndidzakulemekezani ndi milomo yakupfuula mokondwera;
6. Pokumbukira Inu pa kama wanga,Ndi kulingalira za Inu maulonda a usiku.
7. Pakuti munakhala mthandizi wanga;Ndipo ndidzapfuula mokondwera mu mthunzi wa mapiko anu.
8. Moyo wanga uumirira Inu:Dzanja lamanja lanu lindigwiriziza.
9. Koma iwo amene afuna moyo wanga kuti auononge,Adzalowa m'munsi mwace mwa dziko.
10. Adzawapereka ku mphamvu ya lupanga;Iwo adzakhala gawo la ankhandwe.
11. Koma mfumu idzakondwera mwa Mulungu;Yense wakulumbirira iye adzatamandira;Pakuti pakamwa pa iwo onena bodza padzatsekedwa.