Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Masalmo 63:1-4 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

1. Inu Mulungu, ndinu Mulungu wanga; ndidzakufunani m'matanda kuca:Moyo wanga ukumva ludzu la kwa Inu, thupi langa lilirira Inu,M'dziko louma ndi lotopetsa, lopanda madzi.

2. Kuti ndione mphamvu yanu ndi ulemerero wanu,Monga ndinakuonani m'malo oyera.

3. Pakuti cifundo canu ciposa moyo makomedwe ace;Milomo yanga idzakulemekezani.

4. Potero ndidzakuyamikani m'moyo mwanga;Ndidzakweza manja anga m'dzina lanu.

Werengani mutu wathunthu Masalmo 63