Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Masalmo 60:1-5 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

1. Mwatitaya Mulungu, mwatipasula;Mwakwiya; tibwezereni.

2. Mwagwedeza dziko, mwaling'amba:Konzani ming'alu yace; pakuti ligwedezeka.

3. Mwaonetsa anthu anu zowawa:Mwatimwetsa vinyo wotinjenjemeretsa.

4. Koma mwapatsa mbendera akuopa Inu,Aikweze cifukwa ca coonadi.

5. Kuti okondedwa anu alanditsidwe,Pulumutsani ndi dzanja lanu lamanja, ndipo mutibvomereze.

Werengani mutu wathunthu Masalmo 60