Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Masalmo 59:4-13 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

4. Osawapatsa cifukwa ine, athamanga nadzikonza;Galamukani kukomana nane, ndipo penyani.

5. Ndinu Yehova, Mulungu wa makamu, Mulungu wa Israyeli,Ukani kukazonda amitundu onse:Musacitire cifundo mmodzi yense wakucita zopanda pace monyenga.

6. Abwera madzulo, auwa ngati garu,Nazungulira mudzi.

7. Onani abwetuka pakamwa pao;M'milomo mwao muli lupanga,Pakuti amati, Amva ndani?

8. Koma Inu, Yehova, mudzawaseka;Mudzalalatira amitundu onse.

9. Inu, mphamvu yanga, ndidzakulindirani;Pakuti Mulungu ndiye msanje wanga.

10. Mulungu wa cifundo canga adzandikumika:Adzandionetsa tsoka la adani anga.

11. Musawapheretu, angaiwale anthu anga:Muwabalalitse mwa mphamvu yanu, ndipo muwagwetse,Ambuye, ndinu cikopa cathu.

12. Pakamwa pao acimwa ndi mau onse a pa milomo yao,Potero akodwe m'kudzitamandira kwao,Ndiponso cifukwa ca kutemberera ndi bodza azilankhula.

13. Muwathe mumkwiyo, muwagurule psiti:Ndipo adziwe kuti Mulungu ndiye woweruza m'Yakobo,Kufikira malekezero a dziko la pansi.

Werengani mutu wathunthu Masalmo 59