Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Masalmo 59:13-17 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

13. Muwathe mumkwiyo, muwagurule psiti:Ndipo adziwe kuti Mulungu ndiye woweruza m'Yakobo,Kufikira malekezero a dziko la pansi.

14. Ndipo abwere madzulo, auwe ngati garu,Nazungulire mudzi.

15. Ayendeyende ndi kufuna cakudya,Nacezere osakhuta.

16. Koma ine, ndidzayimbira mphamvu yanu;Inde ndidzayimbitsa cifundo canu mamawa:Pakuti Inu mwakhala msanje wanga,Ndi pothawirapo ine tsiku la nsautso yanga.

17. Ndidzayimbira zakukulemekezani Inu, mphamvu yanga:Pakuti Mulungu ndiye msanje wanga, Mulungu wa cifundo canga.

Werengani mutu wathunthu Masalmo 59