Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Masalmo 57:6-11 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

6. Anandichera ukonde apo ndiyenda;Moyo wanga wawerama:Anandikumbira mbuna patsogolo panga;Anagwa m'kati mwace iwo okha.

7. Mtima wanga wakhazikika, Mulungu, ndakhazika mtima;Ndidzayimba, inde, ndidzayimba zolemekeza.

8. Galamuka, ulemu wanga; galamukani cisakasa ndi zeze:Ndidzauka ndekha mamawa.

9. Ndidzakuyamikirani mwa anthu, Ambuye:Ndidzakuyimbirani mwa mitundu.

10. Pakuti cifundo canu ncacikuru kufikira m'mwamba,Ndi coonadi canu kufikira mitambo.

11. Kwezekani m'mwambamwamba, Mulungu;Ulemerero wanu ukhale pamwamba m'dziko lonse lapansi.

Werengani mutu wathunthu Masalmo 57