Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Masalmo 56:2-13 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

2. Adani anga afuna kundimeza tsiku lonse:Pakuti ambiri andithira nkhondo modzikuza.

3. Tsiku lakuopa ine,Ndidzakhulupirira Inu.

4. Mwa Mulungu ndidzalemekeza mau ace:Ndakhulupirira Mulungu, sindidzaopa;Anthu adzandicitanji?

5. Tsiku lonse atenderuza mau anga:Zolingirira zao zonse ziri pa ine kundicitira coipa.

6. Amemezana, alalira,Achereza mapazi anga,Popeza alindira moyo wanga.

7. Kodi adzapulumuka ndi zopanda pace?Gwetsani anthu mumkwiyo, Mulungu.

8. Muwerenga kuthawathawa kwanga:Sungani misozi yanga m'nsupa yanu;Kodi siikhala m'buku mwanu?

9. Pamenepo adani anga adzabwerera m'mbuyo tsiku lakuitana ine:Ici ndidziwa, kuti Mulungu abvomerezana nane.

10. Mwa Mulungu ndidzalemekeza mau ace:Mwa Yehova ndidzalemekeza mau ace.

11. Pa Mulungu ndakhulupirira, sindidzaopa;Munthu adzandicitanji?

12. Zowindira Inu Mulungu, ziri pa ine:Ndidzakucitirani zoyamika.

13. Pakuti mwalanditsa moyo wanga kuimfa:Simunatero nao mapazi anga kuti ndingagwe?Kuti ndiyende pamaso pa MulunguM'kuunika kwa amoyo.

Werengani mutu wathunthu Masalmo 56