Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Masalmo 55:5-11 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

5. Mantha ndi kunjenjemera zandidzera,Ndipo zoopsetsa zandikuta.

6. Ndipo ndinati, Ha, wina akadandipatsa mapiko onga a njiwaMwenzi nditauluka, ndi kukhaliratu.

7. Onani, ndikadathawira kutari,Ndikadagona m'cipululu.

8. Ndikadafulumira ndipulumukeKu mphepo yolimba ndi namondwe.

9. Aonongeni, Ambuye, gawani lilime lao:Pakuti ndaona ciwawa ndi ndeu m'mudzimo.

10. Izizo ziuzungulira pa malinga ace usana ndi usiku;Ndipo m'kati mwace muli zapanda pace ndi cobvuta.

11. M'kati mwace muli kusakaza:Ciwawa ndi cinyengo sizicoka m'makwalala ace.

Werengani mutu wathunthu Masalmo 55