16. Koma ine ndidzapfuulira kwa Mulungu;Ndipo Yehova atizandipulumutsa.
17. Madzulo, m'mawa, ndi msana ndidzadandaula, ndi kubuula,Ndipo adzamva mau anga.
18. Anaombola moyo wanga ku nkhondo yondilaka, ndikhale mumtendere:Pakuti ndiwo ambiri okangana nane.
19. Mulungu adzamva, nadzawasautsa,Ndiye wokhalabe ciyambire kale lomwe.Popeza iwowa sasinthika konse,Ndipo saopa Mulungu.
20. Anaturutsa manja ace awagwire iwo akuyanjana naye:Anaipsa pangano lace.