Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Masalmo 55:1-7 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

1. Cherani khutu pemphero langa, Mulungu;Ndipo musadzibisa pa kupemba kwanga.

2. Mveram, ndipo mundiyankhe:Ndiliralira m'kudandaula kwanga ndi kubuula;

3. Cifukwa ca mau a mdani,Cifukwa ca kundipsinja woipa;Pakuti andisenza zopanda pace,Ndipo adana nane mumkwiyo.

4. Mtima wanga uwawa m'kati mwanga;Ndipo zoopsa za imfa zandigwera.

5. Mantha ndi kunjenjemera zandidzera,Ndipo zoopsetsa zandikuta.

6. Ndipo ndinati, Ha, wina akadandipatsa mapiko onga a njiwaMwenzi nditauluka, ndi kukhaliratu.

7. Onani, ndikadathawira kutari,Ndikadagona m'cipululu.

Werengani mutu wathunthu Masalmo 55