Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Masalmo 55:1-14 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

1. Cherani khutu pemphero langa, Mulungu;Ndipo musadzibisa pa kupemba kwanga.

2. Mveram, ndipo mundiyankhe:Ndiliralira m'kudandaula kwanga ndi kubuula;

3. Cifukwa ca mau a mdani,Cifukwa ca kundipsinja woipa;Pakuti andisenza zopanda pace,Ndipo adana nane mumkwiyo.

4. Mtima wanga uwawa m'kati mwanga;Ndipo zoopsa za imfa zandigwera.

5. Mantha ndi kunjenjemera zandidzera,Ndipo zoopsetsa zandikuta.

6. Ndipo ndinati, Ha, wina akadandipatsa mapiko onga a njiwaMwenzi nditauluka, ndi kukhaliratu.

7. Onani, ndikadathawira kutari,Ndikadagona m'cipululu.

8. Ndikadafulumira ndipulumukeKu mphepo yolimba ndi namondwe.

9. Aonongeni, Ambuye, gawani lilime lao:Pakuti ndaona ciwawa ndi ndeu m'mudzimo.

10. Izizo ziuzungulira pa malinga ace usana ndi usiku;Ndipo m'kati mwace muli zapanda pace ndi cobvuta.

11. M'kati mwace muli kusakaza:Ciwawa ndi cinyengo sizicoka m'makwalala ace.

12. Pakuti si mdani amene ananditonzayo;Pakadatero ndikadacilola:Amene anadzikuza pa ine sindiye munthu wondida;Pakadatero ndikadambisalira:

13. Koma ameneyo ndiwe, munthu woyenerana nane,Tsamwali wanga, wodziwana nane.

14. Tinapangirana upo wokoma,Tinaperekeza khamu la anthu popita ku nyumba ya Mulungu.

Werengani mutu wathunthu Masalmo 55