Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Masalmo 5:8-12 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

8. Yehova, munditsogolere m'cilungamo canu, cifukwa ca akundizondawo;Mulungamitse njira yanu pamaso panga.

9. Pakuti m'kamwa mwao mulibe mau okhazikika;M'kati mwao m'mosakaza;M'mero mwao ndi manda apululu:Lilime lao asyasyalika nalo.

10. Muwayese otsutsika Mulungu;Agwe nao uphungu wao:M'kucuruka kwa zolakwa zao muwapitikitse;Pakuti anapikisana ndi Inu.

11. Koma akondwere onse amene athawira kwa Inu,Apfuule mokondwera kosaleka, popeza muwafungatira;Nasekere mwa Inu iwo akukonda dzina lanu.

12. Pakuti Inu, Yehova, mudzadalitsa wolungamayo;Mudzamcinjiriza naco cibvomerezo ngati cikopa.

Werengani mutu wathunthu Masalmo 5