Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Masalmo 5:4-8 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

4. Pakuti Inu sindinu Mulungu wakukondwera naco coipaMphulupulu siikhala ndi Inu.

5. Opusa sadzakhazikika pamaso panu:Mudana nao onse akucita zopanda pace.

6. Mudzaononga iwo akunena bodza:Munthu wokhetsa mwazi ndi wacinyengo, Yehova anyansidwa naye.

7. Koma ine, mwa kucuruka kwa cifundo canu ndidzalowa m'nyumba yanu:Ndidzagwada kuyang'ana Kacisi wanu woyera ndi kuopa Inu.

8. Yehova, munditsogolere m'cilungamo canu, cifukwa ca akundizondawo;Mulungamitse njira yanu pamaso panga.

Werengani mutu wathunthu Masalmo 5