Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Masalmo 48:7-14 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

7. Muswa zombo za ku Tarisi ndi mphepo ya kum'mawa.

8. Monga tidamva, momwemo tidapenyaM'mudzi wa Yehova wa makamu, m'mudzi wa Mulungu wathu:Mulungu adzaukhazikitsa ku nthawi yamuyaya.

9. Tidalingalira za cifundo canu, Mulungu,M'kati mwa Kacisi wanu.

10. Monga dzina lanu, Mulungu,Momwemo lemekezo lanu ku malekezero a dziko lapansi:M'dzanja lamanja lanu mudzala cilungamo.

11. Likondwere phiri la Ziyoni,Asekere ana akazi a Yuda,Cifukwa ca maweruzo anu.

12. Zungulirani Ziyoni, ndipo muuzinge;Werengani nsanja zace.

13. Penyetsetsani malinga ace,Yesetsani zinyumba zace;Kuti mukaziwerengere mibadwo ikudza m'mbuyo.

14. Pakuti Mulungu ameneyo ndiye Mulungu wathu ku nthawi za nthawi:Adzatitsogolera kufikira imfa.

Werengani mutu wathunthu Masalmo 48