Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Masalmo 48:5-12 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

5. Anapenya mudziwo, ndipo pamenepo anadabwa;Anaopsedwa, nathawako.

6. Pomwepo anagwidwa nako kunthunthumira;Anamva cowawa, ngati wam'cikuta.

7. Muswa zombo za ku Tarisi ndi mphepo ya kum'mawa.

8. Monga tidamva, momwemo tidapenyaM'mudzi wa Yehova wa makamu, m'mudzi wa Mulungu wathu:Mulungu adzaukhazikitsa ku nthawi yamuyaya.

9. Tidalingalira za cifundo canu, Mulungu,M'kati mwa Kacisi wanu.

10. Monga dzina lanu, Mulungu,Momwemo lemekezo lanu ku malekezero a dziko lapansi:M'dzanja lamanja lanu mudzala cilungamo.

11. Likondwere phiri la Ziyoni,Asekere ana akazi a Yuda,Cifukwa ca maweruzo anu.

12. Zungulirani Ziyoni, ndipo muuzinge;Werengani nsanja zace.

Werengani mutu wathunthu Masalmo 48