Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Masalmo 47:2-9 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

2. Pakuti Yehova Wam'mwambamwamba ndiye woopsa;Ndiye mfumu yaikuru pa dziko lonse lapansi.

3. Atigonjetsera anthu,Naika amitundu pansi pa mapazi athu.

4. Atisankhira colowa cathu,Cokometsetsa ca Yakobo amene anamkonda.

5. Mulungu wakwera ndi mpfuu,Yehova ndi liu la lipenga.

6. Yimbirani Mulungu, yimbirani;Yimbirani Mfumu yathu, yimbirani.

7. Pakuti Mulungu ndiye Mfumu ya dziko lonse lapansi;Yimbirani ndi cilangizo.

8. Mulungu ndiye Mfumu ya amitundu:Mulungu akhala pa mpando wacifumu wace woyera.

9. Akulu a anthu asonkhanaAkhale anthu a Mulungu wa Abrahamu:Pakuti zikopa za dziko lapansi nza Mulungu;Akwezeka kwakukuru Iyeyo.

Werengani mutu wathunthu Masalmo 47