Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Masalmo 44:4-11 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

4. Inu ndinu mfumu yanga, Mulungu:Lamulirani cipulumutso ca Yakobo.

5. Mwa Inu tidzakankhira pansi otsutsana nafe:M'dzina lanu tidzapondereza akutiukira ife.

6. Pakuti sinditama uta wanga,Ndipo lupanga langa silingandipulumutse.

7. Koma Inu munatipulumutsa kwa iwo akutsutsana nafe,Ndipo akudana nafe, mudawacititsa manyazi.

8. Mwa Mulungu tidzitamanda tsiku lonse,Ndipo dzina lanu tidzaliyamika kosatha.

9. Koma mwatitaya, ndi kutinyazitsa;Ndipo simuturuka nao makamu a nkhondo athu.

10. Mutibwereretsa kuthawa otisautsa:Ndipo akudana nafe adzifunkhira okha.

11. Mwatipereka ngati nkhosa zoyenera kuzidya;Ndipo mwatibalalitsa mwa amitundu.

Werengani mutu wathunthu Masalmo 44