Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Masalmo 44:12-25 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

12. Mugulitsa anthu anu kwacabe,Ndipo mtengo wace simupindula nao.

13. Mutisandutsa cotonza kwa anzathu,Ndi coseketsa ndi colalatitsa iwo akutizinga.

14. Mutiika tikhale onyozeka mwa amitundu,Ndi kuti anthu atipukusire mitu.

15. Tsiku lonse cimpepulo canga cikhala pamaso panga,Ndipo manyazi a pankhope panga andikuta.

16. Cifukwa ca mau a wotonza wocitira mwano;Cifukwa ca mdani ndi wobwezera cilango,

17. Zonsezi zatigwera; koma sitinakuiwalani,Ndipo sitinacita monyenga m'pangano lanu.

18. Mtima wathu sunabwerera m'mbuyo,Ndipo m'mayendedwe athu sitinapatuka m'njira yanu;

19. Mungakhale munatityola mokhala zirombo,Ndi kutiphimba nao mthunzi wa imfa.

20. Tikadaiwala dzina la Mulungu wathu,Ndi kutambasulira manja athu kwa mulungu wacilendo;

21. Mulungu sakadasanthula ici kodi?Pakuti adziwa zinsinsi za mtima.

22. Koma, cifukwa ca Inu, tiphedwa tsiku lonse;Tiyesedwa ngati nkhosa zakuzipha.

23. Galamukani, mugoneranji, Ambuye?Ukani, musatitaye citayire.

24. Mubisiranji nkhope yanu,Ndi kuiwala kuzunzika ndi kupsinjika kwathu?

25. Pakuti moyo wathu waweramira kupfumbi:Pamimba pathu pakangamira dziko lapansi.

Werengani mutu wathunthu Masalmo 44