Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Masalmo 36:1-12 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

1. Colakwa ca woipayo cimati m'kati mwa mtima wanga,Palibe kuopa Mulungu pamaso pace.

2. Pakud adzidyoletsa yekha m'kuona kwace,Kuti anthu sadzacipeza coipa cace ndi kukwiya naco.

3. Mau a pakamwa pace ndiwo opanda pace ndi onyenga:Waleka kuzindikira ndi kucita bwino.

4. Alingirira zopanda pace pakama pace;Adziika panjira posad pabwino;Coipa saipidwa naco.

5. Yehova, m'mwambamuli cifundo canu;Coonadi canu cifikira kuthambo.

6. Cilungamo canu cikunga mapiri a Mulungu;Maweruzo anu akunga cozama cacikuru:Yehova, musunga munthu ndi nyama.

7. Ha! cifundo canu, Mulungu, ncokondedwadi!Ndipo ana a anthu athawira ku mthunzi wa mapiko anu.

8. Adzakhuta kwambiri ndi zonona za m'nyumba mwanu:Ndipo mudzawamwetsa mu mtsinje wa zokondweretsa zanu.

9. Pakuti citsime ca moyo ciri ndi Inu:M'kuunika kwanu tidzaona kuunika.

10. Tanimphitsani cifundo canu pa iwo akudziwa Inu;Ndi cilungamo canu pa oongoka mtima.

11. Phazi la akudzikuza lisandifikire ine,Ndi dzanja la oipa lisandicotse.

12. Pomwepo padagwera ocita zopanda pace:Anawalikha, ndipo sadzatha kuukanso.

Werengani mutu wathunthu Masalmo 36