Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Masalmo 35:22-28 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

22. Yehova, mudacipenya; musakhale cete:Ambuye, musakhale kutali ndi ine.

23. Galamukani, ndipo khalani maso kundiweruzira mlandu wanga,Mulungu wanga ndi Ambuye wanga,

24. Mundiweruze monga mwa cilungamo canu, Yehova Mulungu wanga;Ndipo asandisekerere ine.

25. Asanene mumtima mwao, Hede, momwemo!Asanene, Tammeza iye.

26. Acite manyazi, nadodome iwo akukondwera cifukwa ca coipa cidandigwera:Abvekeke ndi manyazi ndi kupunzika iwo akudzikuza pa ine.

27. Apfuule mokondwera nasangalale iwo akukondwera naco cilungamo canga:Ndipo anene kosalekeza, Abuke Yehova,Amene akondwera ndi mtendere wa mtumiki wace.

28. Ndipo lilime langa lilalikire cilungamo canu,Ndi lemekezo lanu tsiku lonse.

Werengani mutu wathunthu Masalmo 35