19. Adani anga asandikondwerere ine monyenga;Okwiya nane kopanda cifukwa asanditsinzinire.
20. Pakuti salankhula zamtendere:Koma apangira ciwembu odekha m'dziko.
21. Ndipo andiyasamira m'kamwa mwao;Nati, Hede, Hede, diso lathu lidacipenya.
22. Yehova, mudacipenya; musakhale cete:Ambuye, musakhale kutali ndi ine.
23. Galamukani, ndipo khalani maso kundiweruzira mlandu wanga,Mulungu wanga ndi Ambuye wanga,
24. Mundiweruze monga mwa cilungamo canu, Yehova Mulungu wanga;Ndipo asandisekerere ine.