Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Masalmo 35:19-24 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

19. Adani anga asandikondwerere ine monyenga;Okwiya nane kopanda cifukwa asanditsinzinire.

20. Pakuti salankhula zamtendere:Koma apangira ciwembu odekha m'dziko.

21. Ndipo andiyasamira m'kamwa mwao;Nati, Hede, Hede, diso lathu lidacipenya.

22. Yehova, mudacipenya; musakhale cete:Ambuye, musakhale kutali ndi ine.

23. Galamukani, ndipo khalani maso kundiweruzira mlandu wanga,Mulungu wanga ndi Ambuye wanga,

24. Mundiweruze monga mwa cilungamo canu, Yehova Mulungu wanga;Ndipo asandisekerere ine.

Werengani mutu wathunthu Masalmo 35