Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Masalmo 35:17-28 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

17. Ambuye, mudzapenyerabe nthawi yanji?Bwezani moyo wanga kwa zakundiononga zao,Wanga wa wokha kwa misona ya mkango.

18. Ndidzakuyamikanimumsonkhano waukuru:M'cikhamu ca anthu ndidzakulemekezani.

19. Adani anga asandikondwerere ine monyenga;Okwiya nane kopanda cifukwa asanditsinzinire.

20. Pakuti salankhula zamtendere:Koma apangira ciwembu odekha m'dziko.

21. Ndipo andiyasamira m'kamwa mwao;Nati, Hede, Hede, diso lathu lidacipenya.

22. Yehova, mudacipenya; musakhale cete:Ambuye, musakhale kutali ndi ine.

23. Galamukani, ndipo khalani maso kundiweruzira mlandu wanga,Mulungu wanga ndi Ambuye wanga,

24. Mundiweruze monga mwa cilungamo canu, Yehova Mulungu wanga;Ndipo asandisekerere ine.

25. Asanene mumtima mwao, Hede, momwemo!Asanene, Tammeza iye.

26. Acite manyazi, nadodome iwo akukondwera cifukwa ca coipa cidandigwera:Abvekeke ndi manyazi ndi kupunzika iwo akudzikuza pa ine.

27. Apfuule mokondwera nasangalale iwo akukondwera naco cilungamo canga:Ndipo anene kosalekeza, Abuke Yehova,Amene akondwera ndi mtendere wa mtumiki wace.

28. Ndipo lilime langa lilalikire cilungamo canu,Ndi lemekezo lanu tsiku lonse.

Werengani mutu wathunthu Masalmo 35