Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Masalmo 35:1-7 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

1. Tsutsanani nao iwo akutsutsana nane, Yehova:Limbanani nao iwo akulimbana nane.

2. Gwirani cikopa cocinjiriza, Ukani kundithandiza.

3. Sololani nthungo, ndipo muwatsekerezere kunjira akundilondola:Nenani ndi moyo wanga, Cipulumutso cako ndine.

4. Athe nzeru nacite manyazi iwo akufuna moyo wanga:Abwezedwe m'mbuyo nasokonezeke iwo akundipangira ciwembu.

5. Akhale monga mungu kumphepo,Ndipo mngelo wa Yehova awapitikitse.

6. Njira yao ikhale ya mdima ndi yoterera,Ndipo mngelo wa Yehova awalondole.

7. Pakuti anandichera ukonde wao m'mbunamo kopanda cifukwa,Anakumbira moyo wanga dzenje kopanda cifukwa.

Werengani mutu wathunthu Masalmo 35