9. Pakuti ananena, ndipo cinacitidwa;Analamulira, ndipo cinakhazikika.
10. Yehova aphwanya upo wa amitundu:Asandutsa cabe zolingirira za mitundu ya anthu.
11. Ciweruzo ca Yehova cikhazikika cikhazikikire,Zolingirira za m'mtima mwace ku mibadwo mibadwo.
12. Wodalitsika mtundu wa anthu umene Yehova ndiye Mulungu wao;Mtundu womwe anausankha ukhale colandira ca iye yekha.
13. Yehova apenyerera m'mwamba; Aona ana onse a anthu.
14. M'malo akhalamo Iye, amapenya pansiPa onse akukhala m'dziko lapansi;
15. Iye amene akonza mitima ya iwo onse,Amene azindikira zocita zao zonse.