Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Masalmo 33:7-19 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

7. Amaunjika madzi a m'nyanja monga mulu:Amakundika zakudya mosungiramo.

8. Dziko lonse lapansi liope Yehova:Ponse pali anthu acite mantha cifukwa ca Iye,

9. Pakuti ananena, ndipo cinacitidwa;Analamulira, ndipo cinakhazikika.

10. Yehova aphwanya upo wa amitundu:Asandutsa cabe zolingirira za mitundu ya anthu.

11. Ciweruzo ca Yehova cikhazikika cikhazikikire,Zolingirira za m'mtima mwace ku mibadwo mibadwo.

12. Wodalitsika mtundu wa anthu umene Yehova ndiye Mulungu wao;Mtundu womwe anausankha ukhale colandira ca iye yekha.

13. Yehova apenyerera m'mwamba; Aona ana onse a anthu.

14. M'malo akhalamo Iye, amapenya pansiPa onse akukhala m'dziko lapansi;

15. Iye amene akonza mitima ya iwo onse,Amene azindikira zocita zao zonse.

16. Palibe mfumu yoti gulu lalikuru limpulumutsa:Mphamvu yaikuru siicilanditsa ciphona,

17. Kavalo safikana kupulumuka naye:Cinkana mphamvu yace njaikuru sapulumutsa.

18. Taonani, diso la Yehova liri pa iwo akumuopa Iye,Pa iwo akuyembekeza cifundo cace;

19. Kupulumutsa moyo wao kwa imfa,Ndi kuwasunga ndi moyo m'nyengo ya njala.

Werengani mutu wathunthu Masalmo 33