Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Masalmo 33:17-22 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

17. Kavalo safikana kupulumuka naye:Cinkana mphamvu yace njaikuru sapulumutsa.

18. Taonani, diso la Yehova liri pa iwo akumuopa Iye,Pa iwo akuyembekeza cifundo cace;

19. Kupulumutsa moyo wao kwa imfa,Ndi kuwasunga ndi moyo m'nyengo ya njala.

20. Moyo wathu walindira Yehova:Iye ndiye thandizo lathu ndi cikopa cathu.

21. Pakuti mtima wathu udzakondwera mwa Iye,Cifukwa takhulupirira dzina lace loyera.

22. Yehova, cifundo canu cikhale pa ife,Monga takuyembekezani Inu.

Werengani mutu wathunthu Masalmo 33