11. Ciweruzo ca Yehova cikhazikika cikhazikikire,Zolingirira za m'mtima mwace ku mibadwo mibadwo.
12. Wodalitsika mtundu wa anthu umene Yehova ndiye Mulungu wao;Mtundu womwe anausankha ukhale colandira ca iye yekha.
13. Yehova apenyerera m'mwamba; Aona ana onse a anthu.
14. M'malo akhalamo Iye, amapenya pansiPa onse akukhala m'dziko lapansi;
15. Iye amene akonza mitima ya iwo onse,Amene azindikira zocita zao zonse.
16. Palibe mfumu yoti gulu lalikuru limpulumutsa:Mphamvu yaikuru siicilanditsa ciphona,
17. Kavalo safikana kupulumuka naye:Cinkana mphamvu yace njaikuru sapulumutsa.
18. Taonani, diso la Yehova liri pa iwo akumuopa Iye,Pa iwo akuyembekeza cifundo cace;