Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Masalmo 33:1-6 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

1. Pfuulani mokondwera mwa Yehova, inu olungama mtima:Oongoka mtima ayenera kulemekeza.

2. Yamikani Yehova ndi zeze:Myimbireni ndi cisakasa ca zingwe khumi.

3. Mumyimbire Iye Nyimbo yatsopano;Muyimbe mwaluso kumveketsa mau.

4. Pakuti mau a Yehova ali olunjika;Ndi nchito zace zonse zikhulupirika.

5. Iye ndiye wakukonda cilungamo ndi ciweruzo:Dziko lapansi ladzala ndi cifundo ca Yehova.

6. Zakumwamba zinalengedwa ndi mau a Yehova;Ndipo ndi mpweya wa m'kamwa mwace khamu lao lonse.

Werengani mutu wathunthu Masalmo 33