7. Ndidzakondwera ndi kusangalala m'cifundo canu:Pakuti mudapenya zunzo langa;Ndipo mudadziwa mzimu wanga mu nsautso yanga:
8. Ndipo simunandipereka m'dzanja la mdani;Munapondetsa mapazi anga pali malo.
9. Mundicitire cifundo, Yehova, pakuti ndasautsika ine:Diso langa, mzimu wanga, ndi mimba yanga, zapuwala ndi mabvuto,
10. Pakuti moyo wanga watha ndi cisoni, ndi zaka zanga zatha ndi kuusa moyo:Mphamvu yanga yafoka cifukwa ca kusakaza kwanga, ndi mafupa anga apuwala.
11. Ndakhala cotonza cifukwa ca akundisautsa onse,Inde, koposa kwa anansi anga; ndipo anzanga andiyesa coopsa:Iwo akundipenya pabwalo anandithawa.
12. Ndaiwalika m'mtima monga wakufa:Ndikhala monga cotengera cosweka.
13. Pakuti ndamva ugogodi wa ambiri,Mantha andizinga:Pondipangira ciwembu,Anatsimikiza mtima kulanda moyo wanga.
14. Koma ine ndakhulupirira Inu, Yehova:Ndinati, Inu ndinu Mulungu wanga,
15. Nyengo zanga ziri m'manja mwanu:Mundilanditse m'manja a adani anga, ndi kwa iwo akundilondola ine.
16. Walitsani nkhope yanu pa mtumiki wanu:Mundipulumutse ndi cifundo canu.