Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Masalmo 31:19-24 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

19. Ha! kukoma kwanu ndiko kwakukuru nanga, kumene munasungira iwo akuopa Inu,Kumene munacitira iwo akukhulupirira Inu, pamaso pa ana a anthu!

20. Pobisalira pamaso panu mudzawabisa kwa ciwembu ca munthu:Mudzawabisa iwo mumsasa kuti muwalanditse pa kutetana kwa malilime.

21. Wolemekezeka Yehova:Pakuti anandicitira cifundo cace codabwiza m'mudzi walinga.

22. Ndipo ine, pakutenga nkhawa, ndinati, Ndadulidwa kundicotsa pamaso panu:Komatu munamva mau a kupemba kwanga pamene ndinapfuulira kwa Inu.

23. Kondani Yehova, Inu nonse okondedwa ace:Yehova asunga okhulupirika,Ndipo abwezera zocuruka iye wakucita zodzitama.

24. Limbikani, ndipo Iye adzalimbitsa mtima wanu,Inu nonse akuyembekeza Yehova.

Werengani mutu wathunthu Masalmo 31