Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Masalmo 31:18-24 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

18. Ikhale yosalankhula milomo ya mabodza,Imene imalankhula mwacipongwe pa olungama mtima,Ndi kudzikuza ndi kunyoza.

19. Ha! kukoma kwanu ndiko kwakukuru nanga, kumene munasungira iwo akuopa Inu,Kumene munacitira iwo akukhulupirira Inu, pamaso pa ana a anthu!

20. Pobisalira pamaso panu mudzawabisa kwa ciwembu ca munthu:Mudzawabisa iwo mumsasa kuti muwalanditse pa kutetana kwa malilime.

21. Wolemekezeka Yehova:Pakuti anandicitira cifundo cace codabwiza m'mudzi walinga.

22. Ndipo ine, pakutenga nkhawa, ndinati, Ndadulidwa kundicotsa pamaso panu:Komatu munamva mau a kupemba kwanga pamene ndinapfuulira kwa Inu.

23. Kondani Yehova, Inu nonse okondedwa ace:Yehova asunga okhulupirika,Ndipo abwezera zocuruka iye wakucita zodzitama.

24. Limbikani, ndipo Iye adzalimbitsa mtima wanu,Inu nonse akuyembekeza Yehova.

Werengani mutu wathunthu Masalmo 31