14. Koma ine ndakhulupirira Inu, Yehova:Ndinati, Inu ndinu Mulungu wanga,
15. Nyengo zanga ziri m'manja mwanu:Mundilanditse m'manja a adani anga, ndi kwa iwo akundilondola ine.
16. Walitsani nkhope yanu pa mtumiki wanu:Mundipulumutse ndi cifundo canu.
17. Yehova, musandicititse manyazi; pakuti ndapfuulira kwa Inu:Oipa acite manyazi, atonthole m'manda.