Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Masalmo 31:13-21 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

13. Pakuti ndamva ugogodi wa ambiri,Mantha andizinga:Pondipangira ciwembu,Anatsimikiza mtima kulanda moyo wanga.

14. Koma ine ndakhulupirira Inu, Yehova:Ndinati, Inu ndinu Mulungu wanga,

15. Nyengo zanga ziri m'manja mwanu:Mundilanditse m'manja a adani anga, ndi kwa iwo akundilondola ine.

16. Walitsani nkhope yanu pa mtumiki wanu:Mundipulumutse ndi cifundo canu.

17. Yehova, musandicititse manyazi; pakuti ndapfuulira kwa Inu:Oipa acite manyazi, atonthole m'manda.

18. Ikhale yosalankhula milomo ya mabodza,Imene imalankhula mwacipongwe pa olungama mtima,Ndi kudzikuza ndi kunyoza.

19. Ha! kukoma kwanu ndiko kwakukuru nanga, kumene munasungira iwo akuopa Inu,Kumene munacitira iwo akukhulupirira Inu, pamaso pa ana a anthu!

20. Pobisalira pamaso panu mudzawabisa kwa ciwembu ca munthu:Mudzawabisa iwo mumsasa kuti muwalanditse pa kutetana kwa malilime.

21. Wolemekezeka Yehova:Pakuti anandicitira cifundo cace codabwiza m'mudzi walinga.

Werengani mutu wathunthu Masalmo 31