Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Masalmo 31:1-10 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

1. Ndakhulupirira Inu, Yehova, ndikhale wopanda manyazi nthawi zonse:Mwa cilungamo canu ndipulumutseni ine.

2. Mundicherere khutu lanu; ndipulumutseni msanga:Mundikhalire ine thanthwe lolimba, nyumba yamalinga yakundisunga.

3. Pakuti Inu ndinu thanthwe langa ndi linga langa;Ndipo cifukwa ca dzina lanu ndiyendetseni bwino, ndipo nditsogolereni.

4. Mundionjole m'ukonde umene anandichera mobisika.Pakuti Inu ndinu mphamvu yanga.

5. Ndipereka mzimu wanga m'dzanja lanu:Mwandiombola, Inu Yehova, Mulungu wa coonadi.

6. Ndikwiya nao iwo akusamala zacabe zonama:Koma ndikhulupirira Yehova.

7. Ndidzakondwera ndi kusangalala m'cifundo canu:Pakuti mudapenya zunzo langa;Ndipo mudadziwa mzimu wanga mu nsautso yanga:

8. Ndipo simunandipereka m'dzanja la mdani;Munapondetsa mapazi anga pali malo.

9. Mundicitire cifundo, Yehova, pakuti ndasautsika ine:Diso langa, mzimu wanga, ndi mimba yanga, zapuwala ndi mabvuto,

10. Pakuti moyo wanga watha ndi cisoni, ndi zaka zanga zatha ndi kuusa moyo:Mphamvu yanga yafoka cifukwa ca kusakaza kwanga, ndi mafupa anga apuwala.

Werengani mutu wathunthu Masalmo 31