Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Masalmo 30:7-12 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

7. Inu, Yehova, munakhazikitsa phiri langa ndi kuyanja kwanu:Munabisa nkhope yanu; ndinaopa.

8. Ndinapfuulira kwa Inu, Yehova;Kwa Yehova ndinapemba:

9. M'mwazi mwanga muli phindu lanji, potsikira ine kudzenje?Ngati pfumbi lidzayamika Inu? ngati lidzalalikira coonadi canu?

10. Mverani, Yehova, ndipo ndicitireni cifundo:Yehova, mundithandize ndi Inu.

11. Munasanduliza kulira kwanga kukhale kusekera;Munandibvula ciguduli canga, ndipo munandibveka cikondwero:

12. Kuti ulemu wanga uyimbire Inu, wosakhala cete.Yehova Mulungu wanga, ndidzakuyamikani nthawi zonse.

Werengani mutu wathunthu Masalmo 30