10. Mverani, Yehova, ndipo ndicitireni cifundo:Yehova, mundithandize ndi Inu.
11. Munasanduliza kulira kwanga kukhale kusekera;Munandibvula ciguduli canga, ndipo munandibveka cikondwero:
12. Kuti ulemu wanga uyimbire Inu, wosakhala cete.Yehova Mulungu wanga, ndidzakuyamikani nthawi zonse.