Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Masalmo 3:1-7 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

1. Yehova! Ha! acuruka nanga akundisautsa ine!Akundiukira ine ndi ambiri.

2. Ambiri amati kwa moyo wanga,Alibe cipulumutso mwa Mulungu.

3. Ndipo Inu Yehova, ndinu cikopa canga;Ulemerero wanga, ndi wondiweramutsa mutu wanga.

4. Ndipfuula kwa Yehova ndi mau anga,Ndipo andiyankha m'phiri lace loyera,

5. Ndinagona ine pansi, ndinagona tulo;Ndinauka; pakuti Yehova anandicirikiza.

6. Sindidzaopa unyinji wa anthu akundizinga ine.

7. Ukani Yehova; ndipulumutseni, Mulungu wanga!Pakuti mwapanda adani anga onse patsaya;Mwawatyola mano oipawo.

Werengani mutu wathunthu Masalmo 3