Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Masalmo 29:1-7 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

1. Perekani kwa Yehova, inu ana a amphamvu,Perekani kwa Yehova ulemerero ndi mphamvu.

2. Perekani kwa Yehova ulemerero wa dzina lace:Gwadirani Yehova moyera ndi mokometsetsa.

3. Liu la Yehova liri pamadzi;Mulungu wa ulemerero agunda,Ndiye Yehova pa madzi ambiri.

4. Liu la Yehova ndi lamphamvu;Liu la Yehova ndi lalikurukuru.

5. Liu la Yehova lithyola mitengo yamkungudza;Inde Yehova athyola mikungudza ya ku Lebano.

6. Aitumphitsa monga mwana wa ng'ombe;Lebano ndi Sirio monga msona wa njati.

7. Liu la Yehova ligawa malawi a moto.

Werengani mutu wathunthu Masalmo 29